Professional Documents
Culture Documents
Chili Kuti
Chili Kuti
NDAKATULO ZINA
By Ridson Sambuka
CHILI KUTI
Alidere ndazindikira.
Kwamazunzo azawoneni
Chilombi chotheratu
Wandisiyira tiwanati
Wapeza tiyendayenda
Chili kuti?
2. ANKATERO NDANI?
Ndikumaseka chikhakhali
Ndikakumbuka zomwe awo ankayankhula
Anazitengera Nanthambwe
Chisatha kwamuyaya
Kam'mwamba katsike
Ndikukanika kusimba
4. TSOGOLO
Kumbali ndinkangowatayira
Ankandinyengeza nditochepa
Tomwe ankandipatsa
Chifukwa sindinkadziwa
Pakhomo panga
Mwazunzika anthuni
Mikwingwirima yosaneneka
6. CHIKONDI
Ndikakhala duu!
Kulingalira za iwe
Ndikumasowa mtendere
Chifukwa Chosakumvetsetsa
Ndiwe yani?
Mikoko yogona
Ngakhalenso chidani
Wabweretsa pamodzi anthu osiyanasiyana
Mbambadi! Ndisaname
Wandigonthetsa m'khutu
Ndiwe yani?
Zimavuta kuwalekanitsa
Imakhala dyokodyoko
Ndiwe yani?
Ndagwidwa njakata
Umafika mosadzindikirika
Ndiwe yani?
7. NDIKADADZIWA
Ndikadangokhala chete!
Osalingalira za iwe
Ndikakhala Phee!
Chikumbumtima chikumandigwira
Ndikadawudulira panjira
Wandikhumudwitsa ndisaname
Ndiwe otani
Ndati ndikadadziwa
Yanga sindikadayitayira pa iwe
Ndipo ndikulakalaka
Nditangokusiya pa mtsika
Aaaa! Ndisaname
Pena ndikumadzifunsa
Ndikumasowa chokamba
Koma ndikadadziwa