You are on page 1of 14

Bungwe la CWO linayamba mu

chaka cha 1974 ku parish ya


Mpingo wa Katolika ya St Pius mu
Archdiocese ya Blantyre.

Tikatengera mbiri, nthawi yomwe


Bungwe la CWO linabadwa inali
nthawi ya Vatican Council 2.
Tikumbukire kuti mpingo wa
Katolika unayambitsidwa ndi Yesu
Khristu amene anauza Petulo kuti
chomwe udzamange padziko
lapansi pano chidzamangidwa ndi
kumwamba komwe choncho
zochitika zonse zomwe
zimachitika mimpingo
amakwaniritsa zomwe Yesu mwini
ana. Nthawi yomwe kumachitika
Vatican Council 2 mpingo
umatdogoleledwa ndi Papa
Yohane 23 amene anatenga udido
kuchokera kwa Papa Pio 12. Papa
Yohane 23 atafika anawona kuti
kamvetsedwe, kachitidwe ndi
kayankhulidwe ka anthu ena
mumpingo zimasokanizika, zia
mwa izo zinali ziphunzitso monga
chokuti Papa akayankhula
wayankhula basi. Izi anthu ena
samazimvetsa bwino choncho
samazilandira bwino ndipo
amazitenga mwachabe ndipo
takula nazo. Mwachitsanzo
Bishop akavala chipewa,
kunyamula ndodo yake
ndikukhala pampando,
akayankhula ndiyekuti anthu
amati Bishop wati...
chimodzimodzi Papa akayankhula
kumakhala kuti wamaliza ndipo
chotsatira ndikumvera basi. Ndiye
Papa Yohane 23 anaganizira kuti
akati 'mpingo ndiyekuti sipapa
ekha ayi komanso onse; mpingo
ndife tonse, ndichifukwa chake mu
mauthenga ake Papa Yohane 23
amalimbikitsa kuti aliyense atenge
mbali poyendetsa mpingo ndipo
gawo la anthu omwe nthawi
imeneyo samatekeseka ndi
zampingo anali amai, mwina
chifukwa chakuti nthawiyo
chikhalidwe chimawaonera pansi
amai ndipo ngati follow up ya
nsonkhano wa Vatican Council 2,
Papa anayamba kuitanitsa
misonkhano ya magulu a Akhristu
eniake yosiyanasiyana yomwe
imachitikira kumaiko
osiyanasiyana
kuphatikizapo ku Africa. Ndipo
nsonkhano oyamba unachitikira
ku Ghana ndipo wachiwiri
unachitikira ku Zambia.

Mu chaka cha 1974, Bambo Allan


Chamgwera (omwe tsopano ndi
Bishop opuma wa Zomba) anali
bambo mfumu wa Parish ya St
Pius ku Soche mu Archdiocese ya
Blantyre. Iwowa adatumizidwa
kukhakhala bambo mfumu
oyamba wa Parish ya St Pius ndi
Ambuye Tennison mu chaka cha
1965 koma panthawiyi bambo
Chamgwera anali akukhala ku C.I
Parish kaamba koti nyumba ya
wansembe inali ikumangidwa
ndipo chaka chomwecho Papa
anasankha Ambuye chiwona
kukhala Auxiliary Bishop wa
Blantyre ndipo kenaka mu 1968
Ambuye Tennison anapuma
udindo ndipo anasiyira Ambuye
James Chiona ngati Bishop wa
Blantyre.

Nthawi imeneyi, Bambo Allan


Chamgwera ali bambo mfumu wa
Parish ya St Pius
anayamba kumawerenga
mozama mfundo za mu
misonkhano ya Vatican Council 1
komanso 2 ndikumaona
ndimomwe zinthu zimachitikira ku
parish yawo. Ndipo iwo akuzukuta
zolembalembazo kunapezeka kuti
a episikopi a ku Malawi nawo
anaganiza zotulutsa
kalata/Pastoral letter yomwe
anaitchula kuti Inunso "Pitani
kumunda wanga". Mau oti Inunso
pitani, akutanthauza kuti pali ena
apita kale ndipo ena sanapite
ndipo mau awa amatanthauzira
kuti "Inunso" (amai) amene
mukusalidwa ndipo
simukutekeseka ndi zampingo
mupite nanunso mukagwire nawo
ntchito ya Mulungu. Ndipo
kutanthauzira kwa kalata imeneyi
ya 'Inunso pitani kumunda
kwanga' ndi chiyambi cha bungwe
la Amai mu Dayosezi ya Blantyre
chifukwa Bambo Chamgwera
anaitanitsa nsonkhano wa parish
Council kuyambira pa 3 August
mpaka pa 5 August 1974
ndicholinga chofuna kufotokozera
kalata ya Inunso pitani
kumunda wanga ndipo pamapeto
pake akhristu anavomereza kuti
amvetsa kalatayo. Pa nthawiyi
akhristu eniake ku St Pius
kuphatikizapo a bulazala omwe
anali pa Pastoral experience
nthawiyo Brother Benito Masuwa
omwe pano ndi wansembe
opuma. Potsatira nsonkhano uwu
akhristu anafunsana kuti
"Titani?"ndipo kuyambira nthawi
imeneyo anthu anasankha
kugwira ntchito kudzera mu
mabungwe ndipo kunabadwa
mabungwe osiyanasiyana pa
parishiyo monga bungwe la
ofalitsa uthenga, olalika, a kwaya
komanso bungwe la amai.
Pamene limayamba nthawi
imeneyi Bungwe la amai linali ndi
amai asanu.

Amai awa (Mai Kataika, Chifukwa,


Mai Mbenjere, Mai Mvumbe ndi
Mai Ndovi) anai 'tamva zonse
zomwe zakambidwa zokhudza
kuitanidwa kwathu kuti tigwire
ntchito mumpingo ndipo ife ngati
amai, gawo lathu likhala kusesa
mu chalichi, izi zinali choncho
chifukwa kufikira nthawi imeneyi
amene amasesa mu chalichi anali
mnyamata otumikira kunyumba ya
ansembe komanso asisitere basi.
Komabe sipokhapo, amai
analonjeza kuti kupatula kusesa
mu chalichi, adzigwiranso ntchito
zina monga kusamalira panja pa
chalichi ndi ntchito zina ndipo
amai asanu aja anayamba
kugwira ntchitoyi.

Izi zikuchitika choncho, Ambuye


Chiona analandira uthenga
wansonkhano wa amai omwe
umayenera kukachitikira Lusaka
m'dziko la Zambia ndipo
atamvetsedwa kuti ku St Pius
amai akumakumana kugwira
ntchito ngati bungwe anapempha
bambo mfumu bambo
Chamgwera kuti apemphe mai
mmodzi kukaimilira anzake ku
nsonkhanowu ndipo mai Kataika
amene panthawiyo amuna awo
amagwira ku Air Malawi
anadzipereka kukachita nawo
nsonkhanowu pogwiritsa ntchito
ndalama zawo. Iwo anapitadi
ndipo atabwera uko
anakapereka lipoti la ulendo wawo
ndi za nsonkhano ku likulu
lampingo ku Catholic Secretariat
ndipo likulu lampingo litamva
mfundo zakunsonkhanowo
linayamba kuthandiza bungweli
ndipo bungweli linayamba kukula.

Pamenepa, likulu lampingo


linapempha amai a ku St Pius kuti
afalitse bungweli ku Dinale ya
Blantyre ndipo izi zinapangitsa
kuti amai ena a ku parish ya
Limbe ayambe nawo. Izi
zinapangitsa kuti Mai Bande a ku
Limbe Cathedral parish omwe pa
nthawiyi amagwira ntchito ku Moni
Magazine nawo ayambe kutenga
mbali pa kuyendetsa bungweli
ndipo nsonkhano wachiwiri wa
bungwe la amai omwe
unakachitikiranso ku Lusaka ku
Zambia anakaimilira ndi Mai
Bande. Ichi chinali chiyambi cha
kufalika kwa bungwe la amai la
Catholic Women Organisation mu
Archdiocese ya Blantyre.

You might also like