Professional Documents
Culture Documents
Zilengezo Ndiponso Zofunika Kukumbukira: Zopita Kwa Akulu
Zilengezo Ndiponso Zofunika Kukumbukira: Zopita Kwa Akulu
August 2023
S-147-23.08-CN
(1) Kuti mudziwe ndalama zomwe mungamasunge, phatikizani "Ndalama zonse
zogwiritsidwa ntchito" [e] zomwe zimalembedwa pa fomu ya Lipoti la Pamwezi
Losonyeza Mmene Ndalama za Mpingo Zayendera (S-30) za miyezi 12 yomwe
yapita. (Musaphatikize ndalama zomwe mwalemba mu Lipoti la Pamwezi Losonyeza
Mmene Ndalama za Mpingo Zayendera zomwe ndi ndalama (1) zomwe mpingo
unagamula kuti ziperekedwe ku ofesi ya nthambi kuti zithandize pa ntchito ya padziko
lonse poona kuti ndalama zonse zimene mpingo ulinazo zachuluka kuposa ndalama
zimene bungwe la akulu likuona kuti ndi zoyenera kusunga, (2) zolipilira ntchito
yokonzanso Nyumba ya Ufumu kapena kukonza zinthu zina zomwe ndalama yake
inachita kutumizidwa kuchokera ku ofesi ya nthambi) Mogwirizana ndi Wetani, mutu
10 komanso Malangizo a Kayendetsedwe ka Ndalama za Mpingo (S-27), ndalama
zowonongedwazo zingaphatikize:
• Ndalama zogwiritsidwa ntchito pa nthawi imene woyang’anira dera
akuchezera mpingo, Ndalamazo zingaphatikizepo zimene anagulira
chakudya, mapepala olembapo zinthu, ndalama zimene anagwiritsa ntchito
poyendera ndiponso ndalama zimene anagwiritsa ntchito pa zinthu zina
zochepa zaumwini.
• Kubwezera ndalama za thiransipoti zimene okamba nkhani amene amabwera
ku mpingo wanu agwiritsa ntchito (kuphatikizapo ndalama za thiransipoti
zimene abale amene achita kutumizidwa ndi ofesi ya nthambi).
• kusindikiza mawu pa mapepala oitanira anthu ku misonkhano, kugula zinthu
zogwiritsa ntchito pamene mpingo ukupanga ulaliki wa m’malo opezeka anthu
ambiri.
• Ngati Nyumba ya Ufumuyo imagwiritsidwa ntchito ndi mpingo umodzi wokha:
Ndalama zowonongedwa pokonzetsa Nyumba ya Ufumu: (1) ndalama
zolipilira madzi, magetsi, intanet kapena zonse zowonongedwa pogwiritsa
ntchito kapena kukonzetsanso Nyumba ya Ufumu, (2) ndalama zimene
wophunzitsa anthu kasamaliridwe ka Nyumba ya Ufumu amagwiritsa ntchito
popita ndi kubwera ku mpingo, monga ndalama zoyendera ndi zogwiritsa
ntchito potumiza ndi kulandira makalata (3) ndalama zowonongedwa
pogwiritsa ntchito komanso kukonza nyumba zina zimene zili pa Nyumba ya
Ufumu.
• Ngati Nyumba ya Ufumuyo imagwiritsidwa ntchito ndi mipingo yoposa iwiri,
amene amalipira zinthu zowonongwedwa pa Nyumba ya Ufumu ndi komiti
yoyang’anira Nyumba ya Ufumu.
• Chigamulo cha ndalama zotumizidwa ku ofesi ya nthambi ku ntchito ya pa
dziko lonse.
(2) Gawani mtengo wa ndalama zonse zowonongedwa zomwe mwaphatikiza ndipo
gawani ndi 12. Mtengo umene mupezewo ukuimira avireji ya ndalama
zowonongedwa mwezi ndi mwezi.
(3) Mungasankhe kuwirikiza kawiri kapena katatu (mtengo wa avireji ya mwezi ndi mwezi
yomwe mwapezayo) kuti muone ndalama zomwe mukufunika kumasunga.
Mwachitsanzo:
Chitani izi poyamba: Ndalama zonse zowonongedwa pa miyezi 12: 12,000
Chitani izi kachiwiri: Gawani mtengowo ndi 12: 1,000
Pomaliza: Wirikizani katatu, izi ndi ndalama zomwe mungamasunge: 3,000
S-147-23.08-CN
7. Nchifukwa chiyani ndi zofunika kukhazikitsa ndalama zofunika kumasunga? (1)
zimathandiza kudziwa ngati mpingo kapena komiti yoyang’anira Nyumba ya Ufumu
ikuyenera kulipira ntchito yokonzetsanso pa Nyumba ya Uufmu kapena ngati ndalamazo
ziyenera kuchokera ku ofesi ya nthambi. (sfl, mu. 21, ndi. 9) (2) kukhazikitsa mtengo wa
ndalama zomwe mpingo ukuyenera kumasunga zimathandiza kuti akulu apange chigamulo
cholondola cha ndalama zomwe angamatumize mwezi ndi mwezi ku ntchito ya pa dziko
lonse ku ofesi ya nthambi. Ngati mpingo sungakwanitse kulipira zonse zowonogedwa pa
ntchito yokonzetsa pa Nyumba ya Ufumu, komanso kulipira zinthu zina za mwezi ndi mwezi
komanso zowonongedwa pa nthawi ya kuchezeredwa ndi woyang’anira dera, zingafunike
kuti akulu akonzetse chigamulo cha zopereka ku ntchito ya pa dziko lonse . — Malangizo a
Kayendetsedwe ka Ndalama za Mpingo (S-27) ndi. 19.
10. Lipoti la Mmene Mpingo Ukuyendera (S-10): Tikukumbutsa akulu kuti adzatumize
fomu ya Lipoti la Mmene Mpingo Ukuyendera (S-10) la chaka cha utumiki cha 2023
pasanadutse pa September 20, pogwiritsa ntchito webusaiti ya JW Hub. Mipingo imene ilibe
S-147-23.08-CN
maakaunti ikhoza kupempha woyang’anira dera wawo kuti adzathandize kutumiza lipoti
lawo, kapena ingatumize pogwiritsa ntchito SMS ku nambala iyi: 84 102 0030.
11. Kuchitira Lipoti Ngozi pa Nyumba ya Ufumu Komanso Malo ena Ochititira Zinthu
Zauzimu: Tikukumbutsa akulu onse kufunika kwa kufufuza mosamala zimene zachititsa
ngozi pamene akudzaza molondola fomu ya Lipoti Lonena za Mavuto a Mwadzidzidzi (TO-
5) nthawi zonse pamene pachitika ngozi pa malo aliwonse olambirira. Cholinga cha kufufuza
zomwe zachititsa ngozi komanso kudzaza fomuyi ndi chofuna kuteteza onse osonkhana
komanso kupeza njira yakuti ngozi ya mtundu umenewo isadzachitike mtsogolo. Pa
chifukwa chimenechi, tikupempha akulu onse kuti nthawi zonse aziona malangizo komanso
mavidiyo amene akupezeka pa JW Hub kuti aone mmene angafufuzire moyenerera zomwe
zachititsa ngozi. Pambuyo pake dzazani fomu ya TO-5 ndipo tumizani ku Setor de Gestão
de Risco ku nthambi, pambuyo pa ngoziyo. Mungapeze malangizo a mmene mungafufuzire
zomwe zachitisa ngozi komanso kudzaza fomu ya TO-5 pa JW Hub popita pa:
• MADOKYUMENTI/ Mavidiyo
• Mmene mungafufuzire pakagwa mavuto a mwadzidzidzi
• Mmene mugalembere Lipoti Lonena za Mavuto a Mwadzidzidzi (TO-5)
• MADOKYUMENTI/ Mafomu
• Instruções para Preencher o Relatório de Incidente de Risco (TO-5i)
Chipwitikizi
• Ndi anthu angati amene sadziwa kuwerenga m’chinenero cha mpingo kapena
zofalitsa zogwiritsidwa ntchito pa misonkhano ya mpingo. Phatikizani ofalitsa, ana
amene amapita ku sukulu komanso onse amene amapezeka pa misonkhano ya
mpingo mokhazikika.
S-147-23.08-CN
Zilengezo Ndiponso Zofunika Kukumbukira
August 2023
ZOPITA KUMIPINGO
1. Ntchito Yapadera Padziko Lonse M’mwezi wa September 2023: Monga m’mene
chilengezo cha m’buyomu chinanenera, m’mwezi wa September 2023, tidzakhala ndi
ntchito yapadera padziko lonse yogawira magazini a Nsanja ya Olonda Na. 2 2020, ya mutu
wakuti; “Kodi Ufumu wa Mulungu N’chiyani? Ofalitsa amene akufuna kudzachita upainiya
othandiza m’mwezi wa September 2023 ali ndi mwayi wodzachita upainiya wa maola 15
kapena 30. Mipingo idzapindula kwambiri ngati akulu adzakhale patsogolo kuchita khama
pa ntchito imeneyi. —Aheb. 13:7.
3. Nkhani Yapadera ya 2024: Pofuna kuti tidzayembekezere ndi chidwi Chikumbutso cha
2024, nkhani yapadera idzakambidwa mlungu woyambira March 11, 2024. Mipingo yomwe
idzakhale ndi msonkhano wadera kapena mlungu wapadera, pa wiki yoyambira March 11,
ndiye kuti nkhani yapadera idzakambidwa kutatsala mlungu umodzi.
4. Chigamulo cha Mwezi ndi Mwezi Chothandiza pa Ntchito Yapadziko Lonse: M’chaka
cha utumiki chikubwerachi, chigamulo chidzaperekedwa ku mpingo chokhudza ndalama
zimene zingamaperekedwe pothandiza pa ntchito ya padziko lonse. Ofesi ya nthambi
imagwiritsa ntchito ndalamazi pothandiza pa zinthu zosiyanasiyana zomwe zimathandiza
mipingo. Zinthu zake ndi monga, kukonzanso komanso kumanga Nyumba za Ufumu, Malo
a Misonkhano, kuthandiza pa zinthu zadzidzidzi zomwe zingachitike pa nyumba za gulu la
Mulungu kuphatikizapo ngozi za m’chilengedwe, ngozi za moto, kubedwa kwa zinthu,
kuwonongedwa kwa katundu wa gulu ndi anthu achiwawa komanso kuthandiza mipingo pa
zinthu zamakono komanso zinthu zina zofanana ndi zimenezi. Ndalamayi imagwiritsi-
dwanso ntchito pothandizira mayendedwe a abale amene akuchita utumiki wa nthawi zonse
amene akufuna kukachita nawo msonkhano wamayiko. [Ngati bungwe la akulu lagwirizana
kuti pakhale chigamulo cha ndalama zimene zingamaperekedwe, mogwirizana ndi
chilengezo chopita ku mabungwe a akulu, ndiye kuti chilengezocho chikuyenera
kulengezedwa panopa. Kapena mungadziwitse mpingo kuti chigamulo chidzaperekedwa
wiki yotsatira.]
S-147-23.08-CN